13/08/2026
Mitengo ya chimanga yayamba kukwera m'madera osiyanasiyana m'dziko muno kuphatikizapo m'maboma aku chigwa cha mtsinje wa Shire komwe m'misika ina chimangachi chafika K60,000 pa thumba lolemera makilogalamu 50.
Ku Nsanje, chimanga amachigulitsa pa mitengo ya pakati pa K50,000 ndi K55,000 mwezi wathawu, ndipo pano chafika pa K60,000, thumba lolemera makilogalamu 50.
Ku Chikwawa, chimanga m'misika ina amachigulitsa pa mitengo ya pakati pa K45,000 ndi K50,000 mwezi wathawu, koma pano ena akuchigulitsa pa mitengo ya pakati pakati pa K55,000 komanso K60,000 thumba lolemera ma kilogalamu 50.
Mkulu oona za ulimi m'boma la Chikwawa, a Isaac Alli, wati kukwera kwa chimangachi ndi kaamba koti anthu ku chigwa cha m'tsinje wa Shire akudalira chimanga chochokera m'madera ena ponena kuti sanakolole chifukwa cha ng'amba ndi madzi osefukira zomwe zidawononga mbeu.
Padakali pano, m'boma la Ntcheu, mchigawo cha pakati, chimangachi chakwera kufika pa K40,000 thumba lolemera makilogalamu 50 kuchoka pa mitengo ya pakati pa K30,000 ndi K35,000 ndipo m'madera aku mpoto maka ku Mzimba, tsopano chili pa K47,000 kuchoka pa K36,000 thumba lolemera makilogalamu 50.
Source: ZBSNews